Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 8:25-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo mwa kucenjera kwace adzapindulitsa cinyengo m'dzanja mwace, nadzadzikuza m'mtima mwace; ndipo posatekeseka anthu, adzaononga ambiri; adzaukiranso kalonga wa akalonga, koma adzatyoledwa popanda dzanja.

26. Ndipo masomphenya a madzulo ndi mamawa adanenawo ndi oona; koma iwe ubise masomphenyawo, popeza adzacitika atapita masiku ambiri.

27. Ndipo ine Danieli ndinakomoka ndi kudwala masiku ena; pamenepo ndinauka ndi kucita nchito ya mfumu; ndipo ndinadabwa nao masomphenyawo, koma panalibe wakuwazindikiritsa.

Werengani mutu wathunthu Danieli 8