Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 6:15-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma anthu awa anasonkhana kwa mfumu, nati kwa mfumu, Dziwani, mfumu, kuti lamulo la Amedi ndi Aperisi, ndilo kuti coletsa ciri conse ndi lemba liri lonse idazikhazikira mfumu, zisasinthike.

16. Pamenepo inalamula mfumu, ndipo anadza naye Danieli, namponya m'dzenje la mikango. Ndipo mfumu inalankhula, niti kwa Danieli, Mulungu wako amene umtumikira kosalekeza, Iyeyu adzakulanditsa.

17. Ndipo anatenga mwala, nauika pakamwa pa dzenje, niukomera mfumu ndi cosindikizira cace, ndi cosindikizira ca akuru ace, kuti kasasinthike kanthu ka Danieli.

18. Pamenepo mfumu inamuka ku cinyumba cace, nicezera kusala usikuwo, ngakhale zoyimbitsa sanabwera nazo pamaso pace, ndi m'maso mwace munamuumira.

19. Nilawira mamawa mfumu, nimuka mofulumira ku dzenje la mikango.

20. Ndipo poyandikira padzenje inapfuula ndi mau acisoni mfumu, ninena, niti kwa Danieli, Danieli, mnyamata wa Mulungu wamoyo, kodi Mulungu wako, amene umtumikira kosalekeza, wakhoza kukulanditsa kwamikango?

21. Pamenepo Danieli anati kwa mfumu, Mfumu, mukhale ndi moyo cikhalire.

Werengani mutu wathunthu Danieli 6