Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 5:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mfumu Belisazara anakonzera anthu ace akulu cikwi cimodzi madyerero akuru, namwa vinyo pamaso pa cikwico.

2. Belisazara, pakulawa vinyo, anati abwere nazo zotengera za golidi ndi siliva adazicotsa Nebukadinezara atate wace ku Kacisi ali ku Yerusalemu, kuti mfumu ndi akuru ace, akazi ace ndi akazi ace ang'ono, amweremo.

3. Nabwera nazo zotengera zagolidi adazicotsa ku Kacisi wa nyumba ya Mulungu ya ku Yerusalemu, ndipo mfumu ndi akuru ace, akazi ace ndi akazi ace ang'ono, anamweramo.

Werengani mutu wathunthu Danieli 5