Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 4:12-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Masamba ace anali okoma, ndi zipatso zace zinacuruka, ndi m'menemo munali zakudya zofikira onse, nyama za kuthengo zinatsata mthunzi wace, ndi mbalame za m'mlengalenga zinafatsa m'thambi zace, ndi nyama zonse zinadyako.

13. Ndinaona m'masomphenya a m'mtima mwanga pakama panga, taonani, mthenga woyera anatsika kumwamba.

14. Anapfuulitsa, natero, Likhani mtengowo, sadzani nthambi zace, yoyolani masamba ace, mwazani zipatso zace, nyama zicoke pansi pace, ndi mbalame pa nthambi zace.

Werengani mutu wathunthu Danieli 4