Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 3:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. kuti pakumva inu mau a lipenga, citoliro, zeze, sansi, cisakasa, ngoli, ndi zoyimbitsa ziri zonse, mugwadire ndi kulambira fano lagolidi adaliimika mfumu Nebukadinezara;

6. ndipo ali yense wosagwadira ndi kulambira, adzaponyedwa nthawi yomweyo m'kati mwa ng'anjo yotentha yamoto.

7. Potero nthawi yomweyo pakumva anthu onse mau a lipenga, citoliro, zeze, sansi, cisakasa, ndi zoyimbitsa ziri zonse, anthu onse, mitundu ya anthu a manenedwe osiyana, anagwadira, nalambira fano lagolidi adaliimika mfumu Nebukadinezara.

8. Cifukwa cace anayandikira Akasidi ena nthawi yomweyi, naneneza Ayuda.

9. Anayankha, nati kwa mfumu Nebukadinezara, Mfumu, mukhale ndi moyo cikhalire.

10. Inu mfumu mwalamulira kuti munthu ali yense amene adzamva mau a lipenga, citoliro, zeze, sansi, cisakasa, ngoli, ndi zoyimbitsa ziri zonse, agwadire, nalambire fanolo lagolidi;

11. ndi yense wosagwadira ndi kulambiraadzaponyedwa m'kati mwa ng'anjo yotentha yamoto.

Werengani mutu wathunthu Danieli 3