Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 11:40-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Ndipo nthawi yotsiriza mfumu ya kumwela idzalimbana naye, ndi mfumu ya kumpoto idzamdzera ngati kabvumvulu, ndi magareta, ndi apakavalo, ndi zombo zambiri; nadzalowa m'maiko, nadzasefukira ndi kupitirira.

41. Adzalowanso m'dziko lokometsetsalo ndi maiko ambiri adzapasuka; koma opulumuka dzanja lace ndi awa: Edomu, ndi Moabu, ndi oyamba a ana a Amoni.

42. Adzatambalitsiranso dzanja lace kumaiko; dziko la Aigupto lomwe silidzapulumuka.

43. Ndipo adzacita mwamphamvu ndi cuma ca golidi, ndi siliva, ndi zinthu zofunika zonse za Aigupto; Alubi ndi Akusi adzatsata mapazi ace.

44. Koma mbiri yocokera kum'mawa ndi kumpoto idzambvuta; nadzaturuka iye ndi ukali waukuru kupha ndi kuononga konse ambiri.

45. Ndipo adzamanga mahema a nyumba yacifumu yace pakati pa nyanja yamcere ndi phiri lopatulika lofunika; koma adzafikira cimariziro cace wopanda wina wakumthandiza.

Werengani mutu wathunthu Danieli 11