Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 1:4-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. anyamata opanda cirema, a maonekedwe okoma, a luso la nzeru zonse, ocenjera m'kudziwa, a luntha lakuganizira, okhoza kuimirira m'cinyumba ca mfumu; ndi kuti awaphunzitse m'mabuku, ndi manenedwe a Akasidi.

5. Ndipo mfumu inawaikira gawo la cakudya ca mfumu tsiku ndi tsiku, ndi la vinyo wakumwa iye, ndi kuti awalere zaka zitatu, kuti potsiriza pace aimirire pamaso pa mfumu.

6. Mwa awa tsono munali a ana a Yuda, Danieli, Hananiya, Misayeli, ndi Azariya.

7. Ndi mkuru wa adindo anawapatsa maina ena; Danieli anamucha Belitsazara; ndi Hananiya, Sadrake; ndi Misaeli, Mesaki; ndi Azariya, Abedinego.

8. Koma Danieli anatsimikiza mtimti kuti asadzidetse ndi cakudya ca mfumu, kapena ndi vinyo amamwa; cifukwa cace anapempha mkuru wa adindo amlole asadzidetse.

9. Ndipo Mulungu anamkometsera Danieli mtima wa mkuru wa adindo, amcitire cifundo.

10. Nati mkuru wa adindo kwa Danieli. Ine ndiopa mbuyanga mfumu, amene anakuikirani cakudya canu ndi cakumwa canu; pakuti aonerenji nkhope zanu zacisoni zoposa za anyamata olingana ndi inu? momwemo mudzaparamulitsa mutu wanga kwa mfumu.

11. Nati Danieli kwa kapitao, amene mkuru wa adindo adamuikayo ayang'anire Danieli, Hananiya, Misaeli, ndi Azariya,

12. Muyesetu anyamata anu masiku khumi; atipatse zomera m'nthaka tidye, ndi madzi timwe.

Werengani mutu wathunthu Danieli 1