Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Amosi 5:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Namwali wa Israyeli wagwa, sadzaukanso; wagwetsedwa pa nthaka yace, palibe womuutsa.

3. Pakuti atero Ambuye Yehova, M'nyumba ya Israyeli, mudzi woturukamo cikwi cimodzi adzautsalira zana limodzi, ndi uwu woturukamo zana limodzi adzautsalira khumi.

4. Pakuti atero Yehova kwa nyumba ya Israyeli, Mundifunefune Ine, ndipo mudzakhala ndi moyo;

5. koma musamafuna Beteli, kapena kumalowa m'Giligala; musamapita ku Beereseba; pakuti Giligala adzalowadi m'ndende, ndi Beteli adzasanduka cabe.

6. Funani Yehova, ndipo mudzakhala ndi mayo; angabuke ngati moto m'nyumba ya Yosefe, ndipo unganyeke wopanda wakuzima m'Beteli;

7. inu osintha ciweruzo cikhale civumulo, nimugwetsa pansi cilungamo,

Werengani mutu wathunthu Amosi 5