Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Amosi 4:6-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo ine ndakupatsaninso mano oyera m'midzi yanu yonse, ndi kusowa mkate m'malo mwanu monse; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

7. Ndipo Ine ndakumanani mvula, itatsala miyezi itatu isanafika nyengo yakukolola; ndipo ndinabvumbistira mudzi umodzi mvula, osabvumbitsira mudzi wina; munda wina unabvumbidwa mvula, ndi m'munda mosabvumbidwa mvula munafota.

8. M'mwemo midzi iwiri kapena itatu inayenda peyupeyu ku mudzi umodzi kukamwa madzi, koma sanakhuta; koma simunai bwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

9. Ndinakukanthani ndi cinsikwi ndi cinoni; minda yanu yocuruka yamipesa, ndi yamikuyu, ndi yaazitona, yaonongeka ndi cirimamine; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

10. Ndinatumiza mliri pakati panu monga m'Aigupto; anyamata anu ndawapha ndi lupanga, ndi kutenga akavalo anu; ndipo ndinakweretsa kununkha kwa cigono canu kufikitsa kumphuno kwanu; ikoma simunabwerera kudzakwa Ine, ati Yehova.

11. Ndinagubuduza ena mwa inu, monga umo Mulungu anagubuduzira Sodomu ndi Gomora; ndipo inu munali ngati muuni wofumulidwa kumoto; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

12. Cifukwa cace ndidzatero nawe, Israyeli; popeza ndidzakucitira ici, dzikonzeretu kukomana ndi Mulungu wako, Israyeli.

13. Pakuti taona, Iye amene aumba mapiri, nalenga mphepo, nafotokozera munthu maganizo ace, nasanduliza m'mawa ukhale mdima, naponda pa misanje ya dziko lapansi, dzina lace ndiye Yehova Mulungu wamakamu.

Werengani mutu wathunthu Amosi 4