Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Amosi 2:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Moabu, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu asanduke njereza;

2. koma ndidzatumiza moto pa Moabu, udzanyeketsa nyumba zacifumu za Kerioti; ndipo Moabu adzafa ndi phokoso, ndi kupfuula, ndi mau a lipenga;

3. ndipo ndidzalikha woweruza pakati pace, ndi kupha akalonga ace onse, ati Yehova.

4. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Yuda, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza akaniza cilamulo ca Yehova, osasunga malemba ace; ndipo awalakwitsa mabodza ao amene makolo ao anawatsata;

5. koma ndidzatumiza moto pa Yuda, udzanyeketsa nyumba zacifumu za m'Yerusalemu.

6. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Israyeli, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza agulitsa wolungama ndi ndalama, ndi wosowa cifukwa ca nsapato;

7. ndiwo amene aliralira pfumbi lapansi liri pamutu pa wosauka, napotoza njira ya wofatsa; ndipo munthu ndi atate wace amuka kwa namwali yemweyo, kuti aipse dzina langa loyera;

8. nagona pansi pa zopfunda za cikole ku maguwa a nsembe ali onse, ndi m'nyumba ya Mulungu wao akumwa vinyo wa iwo olipitsidwa.

Werengani mutu wathunthu Amosi 2