Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 9:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Davide anati, Kodi atsalako wina wa nyumba ya Sauli, kuti ndimcitire cifundo cifukwa ca Jonatani?

2. Ndipo panali mnyamata wa m'nyumba ya Sauli dzina lace Ziba; ndipo anamuitana iye afike kwa Davide; ndi mfumuyo inanena naye, Iwe ndiwe Ziba kodi? Nati iye, Ndine mnyamata wanu ame.

3. Ndipo mfumu inati, Kodi atsalanso wina wa nyumba ya Sauli kuti ndimuonetsere cifundo ca Mulungu? Ziba nanena ndi mfumu, Aliponso mwana wa Jonatani wopunduka mapazi ace.

4. Ndipo mfumu inanena naye, Ali kuti iyeyo? Ziba nanena kwa mfumu, Onani ali m'nyumba ya Makiri, mwana vya Amiyeli ku Lodebara.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 9