Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 6:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Pamenepo Davide anabwerera kudalitsa nyumba yace. Ndipo Mikala mwana wamkazi wa Sauli anaturukira kwa Davide, nati; Ha! Lero mfumu ya Israyeli inalemekezeka ndithu, amene anabvula lero pamaso pa adzakazi a anyamata ace, monga munthu woluluka abvula wopanda manyazi!

21. Koma Davide ananena ndi Mikala, Ndatero pamaso pa Yehova, amene anandisankha ine ndi kupitirira atate wako ndi banja lace lonse, nandiika ndikhale mtsogoleri wa anthu a Yehova, wa Israyeli, cifukwa cace ndidzasewera pamaso pa Yehova.

22. Ndipo ndidzaonjezanso kukhala ngati munthu woluluka, ndidzakhala wodzicepetsa m'maso a ine mwini; ndipo adzakazi udanenawo, ndi amenewo ndidzalemekezedwa.

23. Ndipo Mikala mwana wamkazi wa Sauli sanaona mwana kufikira tsiku la imfa yace.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 6