Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 24:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. nafika ku Gileadi ndi ku dera la Tatimuhodisi; nafika ku Dani-Jaana ndi kuzungulira, kufikira ku Zidoni,

7. nafika ku linga la Turo ndi ku midzi yonse ya Ahivi ndi ya Akanani; naturukira kumwera kwa Yuda ku Beereseba.

8. Comweco pamene atayenda dziko lonse anafika ku Yerusalemu pakutha miyezi isanu ndi inai, ndi masiku makumi awiri.

9. Ndipo Yoabu anapereka kwa mfumu kucuruka kwa anthu adawawerenga; ndipo m'lsrayeli munali anthu zikwi mazana asanu ndi atatu, ngwazi zosolola lupanga; ndi anthu a Yuda ndiwo zikwi mazana asanu.

10. Pamenepo mtima wa Davide unamtsutsa, atatha kuwerenga anthuwoo Davide nati kwa Yehova, Ndinacimwa kwakukuru ndi cinthu cimene ndinacita; koma tsopano Yehova mucotse mphulupulu ya mnyamata wanu, pakuti ndinacita kopusa ndithu.

11. Ndipo pouka Davide m'mawa mau a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlauli wa Davide, kuti,

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 24