44. Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga;Munandisunga ndikhale mutu wa amitundu;Anthu amene sindinawadziwa adzanditsumikira ine.
45. Alendo adzandigonjera ine,Pakumva za ine, adzandimbera pomwepo.
46. Alendo adzafota,Nadzabwera ndi kunthunthumira oturuka mokwiririka mwao.
47. Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;Ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la cipulumutso canga;
48. Inde Mulungu wakundibwezera cilango ine,Ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.