Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 22:44-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga;Munandisunga ndikhale mutu wa amitundu;Anthu amene sindinawadziwa adzanditsumikira ine.

45. Alendo adzandigonjera ine,Pakumva za ine, adzandimbera pomwepo.

46. Alendo adzafota,Nadzabwera ndi kunthunthumira oturuka mokwiririka mwao.

47. Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;Ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la cipulumutso canga;

48. Inde Mulungu wakundibwezera cilango ine,Ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 22