41. Munatembenuzitsanso adani anga andipatse mbuyo,Kuti ndiwalikhe akudana ndi ine.
42. Anayang'ana iwo, koma panalibe wopulumutsa;Ngakhale kwa Yehova, koma iye sanawayankha.
43. Pomwepo ndinawasansantha asalale ngati pfumbi la padziko,Ndinawapondereza ngati dothi la m'makwalala.
44. Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga;Munandisunga ndikhale mutu wa amitundu;Anthu amene sindinawadziwa adzanditsumikira ine.
45. Alendo adzandigonjera ine,Pakumva za ine, adzandimbera pomwepo.
46. Alendo adzafota,Nadzabwera ndi kunthunthumira oturuka mokwiririka mwao.
47. Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;Ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la cipulumutso canga;
48. Inde Mulungu wakundibwezera cilango ine,Ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.
49. Amene anditurutsa kwa adani anga;Inde mundikweza ine pamwamba pa iwo akundiukira;Mundipulumutsa kwa munthu waciwawa.
50. Cifukwa cace ndidzakuongani Yehova, pakati pa amitundu,Ndipo ndidzayimba zolemekeza dzina lanu.
51. Iye apatsa mfumu yace cipulumutso cacikuru;Naonetsera cifundo wodzozedwa wace,Kwa Davide ndi mbeu yace ku nthawi zonse.