4. Ndidzaitanakwa Yehovaamene ayenera timtamande;Comweco ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.
5. Pakuti mafunde a imfa anandizinga,Mitsinje ya zopanda pace inandiopsa ine.
6. Zingwe za kumanda zinandizingira;Misampha ya imfa inandifikira ine.
7. M'kusauka kwanga ndinaitana kwa Yehova,Inde ndinakuwira kwa Mulungu wanga;Ndipo Iye anamva mau anga ali m'kacisi wace,Ndi kulira kwanga kunafika ku makutuace.
8. Pomwepo dziko linagwedezeka ndi kunthunthumira.Maziko a dziko la kumwamba anasunthikaNagwedezeka, cifukwa iye anakwiya.
9. M'mphuno mwace munaturuka utsi,Ndi moto woturuka m'kamwa mwace unaononga;Makala anayaka nao.
10. Anaweramitsa miyambanso, natsika;Ndipo mdima wandiwe-yani unali pansi pa mapazi ace.
11. Ndipo iye anaberekeka pa Kerubi nauluka;Inde anaoneka pa mapiko a mphepo,
12. Ndipo anayesa mdimawo ngati mahema omzungulira iye,Kusonkhana kwa madzi ndi mitambo yocindikira ya mlengalenga.
13. Ceza ca pamaso paceMakala a mota anayaka,
14. Yehova anagunda kumwamba;Ndipo Wam'mwambamwamba ananena mau ace.
15. Ndipo iye anatumiza mibvi, nawawaza;Mphezi, nawaopsa,
16. Pamenepo m'munsi mwa nyanja munaoneka,Maziko a dziko anaonekera poyera,Ndi mthonzo wa Yehova,Ndi mpumo wa mweya wa m'mphuno mwace.
17. Iye anatumiza kucokera kumwamba nanditenga;Iye ananditurutsa m'madzi akuru;