Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 22:37-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Munakulitsa kulunza kwanga pansi panga,Ndi mapazi anga sanaterereka.

38. Ndinapitikitsa adani anga, ndi kuwaononga;Ndiponso sindinabwerera mpaka nditawatha.

39. Ndinawatha ndi kuwapyoza, kuti sakhoza kuuka,Inde anagwa pansi pa mapazi anga.

40. Pakuti Inu munandimanga m'cuuno ndi mphamvu ya kunkhondo; Munandigonjetsera akundiukira.

41. Munatembenuzitsanso adani anga andipatse mbuyo,Kuti ndiwalikhe akudana ndi ine.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 22