Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 22:34-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Iye asandutsa mapazi ace akunga mapazi a mbawala;Nandiika pa misanje yanga.

35. Iye aphunzitsa manja anga nkhondo;Kotero kuti manja anga alifula uta wamkuwa.

36. Ndiponso munandipatsa cikopa ca cipulumutso canu;Ndi kufatsa kwanu kunandikulitsa.

37. Munakulitsa kulunza kwanga pansi panga,Ndi mapazi anga sanaterereka.

38. Ndinapitikitsa adani anga, ndi kuwaononga;Ndiponso sindinabwerera mpaka nditawatha.

39. Ndinawatha ndi kuwapyoza, kuti sakhoza kuuka,Inde anagwa pansi pa mapazi anga.

40. Pakuti Inu munandimanga m'cuuno ndi mphamvu ya kunkhondo; Munandigonjetsera akundiukira.

41. Munatembenuzitsanso adani anga andipatse mbuyo,Kuti ndiwalikhe akudana ndi ine.

42. Anayang'ana iwo, koma panalibe wopulumutsa;Ngakhale kwa Yehova, koma iye sanawayankha.

43. Pomwepo ndinawasansantha asalale ngati pfumbi la padziko,Ndinawapondereza ngati dothi la m'makwalala.

44. Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga;Munandisunga ndikhale mutu wa amitundu;Anthu amene sindinawadziwa adzanditsumikira ine.

45. Alendo adzandigonjera ine,Pakumva za ine, adzandimbera pomwepo.

46. Alendo adzafota,Nadzabwera ndi kunthunthumira oturuka mokwiririka mwao.

47. Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;Ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la cipulumutso canga;

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 22