Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 22:31-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Kunena za Mulungu, njira yace iri yangwiro;Mau a Yehova anayesedwa; iye ndiye cikopa kwa onse akukhulupirira iye.

32. Pakuti Mulungu ndani, koma Yehova?Ndipo thanthwe ndani, koma Mulungu wathu?

33. Mulungu ndiye Gnga langa lamphamvu;Ndipo iye ayendetsa angwiro mu njira yace.

34. Iye asandutsa mapazi ace akunga mapazi a mbawala;Nandiika pa misanje yanga.

35. Iye aphunzitsa manja anga nkhondo;Kotero kuti manja anga alifula uta wamkuwa.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 22