Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 22:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndi acifundo Inu mudzadzionetsa wacifundo,Ndi munthu wangwiro mudzadzionetsa wangwiro;

27. Ndi oyera mtima mudzadzionetsa woyera mtima;Ndi otsutsatsutsa mudzadzionetsa wopotoza.

28. Ndipo mudzapulumutsa anthu osautsidwa;Koma maso anu ali pa odzikuza kuti muwacepetse.

29. Pakuti Inu ndinu nyali yanga, Yehova;Ndipo Yehova adzaunika mumdima mwanga.

30. Pakuti ndi Inu ndithamangira gulu;Ndi Mulungu wanga ndilumphira linga.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 22