Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 22:15-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo iye anatumiza mibvi, nawawaza;Mphezi, nawaopsa,

16. Pamenepo m'munsi mwa nyanja munaoneka,Maziko a dziko anaonekera poyera,Ndi mthonzo wa Yehova,Ndi mpumo wa mweya wa m'mphuno mwace.

17. Iye anatumiza kucokera kumwamba nanditenga;Iye ananditurutsa m'madzi akuru;

18. Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,Kwa iwo akudana ndi ine; pakuti anandiposa mphamvu,

19. Anandifikira ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga,

20. Iye ananditurutsanso ku malo akuru;Iye anandipulumutsa, cifukwa akondwera ndi ine.

21. Yehova anandibwezera monga mwa colungama canga;Monga mwa kuvera kwa manja anga anandipatsa mphotho.

22. Pakuti ndinasunga njira za Yehova,Osapambukira koipa kusiya Mulungu wanga.

23. Pakuti maweruzo ace onse anali pamaso panga;Ndipo za malemba ace, sindinawapambukira.

24. Ndinakhalanso wangwiro kwa iye,Ndipo ndinadzisunga kusacita kuipa kwanga.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 22