Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 19:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anauza Yoabu, Onani mfumu irikulira misozi, nilira Abisalomu.

2. Ndipo cipulumutso ca tsiku lila cinasandulika maliro kwa anthu onse; pakuti anthu anamva kuti, Mfumu iri ndi cisoni cifukwa ca mwana wace.

3. Ndipo tsiku lija anthu analowa m'mudzi kacetecete, monga azemba anthu akucita manyazi pakuthawa nkhondo.

4. Ndipo mfumu inapfunda nkhope yace, nilira ndi mau okweza, Mwana wanga Abisalomu, Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga,

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 19