Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 12:25-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. natumiza ndi dzanja la Natani mneneriyo, namucha dzina lace Wokondedwa ndi Yehova, cifukwa ca Yehova.

26. Ndipo Yoabu anathira nkhondo pa Raba wa ana a Amoni, nalanda mudzi wacifumu.

27. Yoabu natumiza mithenga kwa Davide nati, Ndaponyana ndi Raba, inde ndalanda mudzi wa pamadzi.

28. Cifukwa cace tsono musonkhanitseanthu otsalawo, nimumangire mudziwo zithando, muulande; kuti ine ndingalande mudziwo, ndipo ungachedwe ndi dzina langa.

29. Ndipo Davide anasonkhanitsa anthu onse, napita ku Raba, naponyana nao, naulanda.

30. Nacotsa korona pa mutu wa mfumu yao; kulemera kwace kunali talente wa golidi; ndipo m'menemo munali miyala ya mtengo wapatali; ndipo anamuika pa mutu wa Davide. Iye naturutsa zofunkha za mudziwo zambirimbiri.

31. Naturutsa anthu a m'mudzimo, nawaceka ndi mipeni ya mana mano, ndi nkhwangwa zacitsulo; nawapsitiriza ndi citsulo, nawapititsa m'ng'anjo yanjerwa; natero ndi midzi yonse ya ana a Amoni. Ndipo Davide ndi anthu onse anabwerera kumka ku Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 12