Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 12:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Ndipo anafika kwa iye nanena naye, Pa mudzi wina panali anthu awiri; wina wolemera, wina wosauka.

2. Wolemerayo anali nazo zoweta zazing'ono ndi zazikuru zambiri ndithu;

3. koma wosaukayo analibe kanthu kena koma kamwana kakakazi ka nkhosa, kamene anakagula ndi kukaweta; ndipo kameneko kanakula naye pamodzi ndi ana ace. Kanadyako cakudya cace ca iye yekha, kanamwera m'cikho ca iye yekha, kanagona pa cifukato cace, ndipo kanali kwa iye ngati mwana wace wamkazi.

4. Ndipo kwa wolemerayo kunafika mlendo, ndipo iye analeka kutengako mwa zoweta zace zazing'ono ndi zazikuru, kuphikira mlendo amene anafika kwa iye, koma anatenga mwana wa nkhosa wa wosaukayo, naphikira munthu amene anafika kwa iye.

5. Pamenepo mkwiyo wa Davide unayaka ndithu pa munthuyo, nati kwa Natani, Pali Yehova, munthu amene anacita ici, ayenera kumupha;

6. ndipo adzabwezera mwa mwana wa nkhosayo ena anai, cifukwa anacita ici osakhala naco cifundo.

7. Ndipo Natani ananena kwa Davide, Munthuyo ndi inu nomwe. Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, Ndinakudzoza ukhale mfumu ya Israyeli, ndinakupulumutsa m'dzanja la Sauli;

8. ndinakupatsa nyumba ya mbuye wako, ndi akazi a mbuye wako pa cifukato cako, ndinakupatsanso nyumba ya Israyeli ndi ya Yuda; ndipo zimenezi zikadakucepera ndikadakuonjezera zina zakuti zakuti.

9. Cifukwa ninji unapeputsa mau a Yehova ndi kucita cimene ciri coipa pamaso pace? Unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndi kutenga mkazi wace akhale mkazi wako; ndipo unamupha iye ndi lupanga la ana a Amoni.

10. Cifukwa cace tsono lupanga silidzacoka pa nyumba yako nthawi zonse, popeza unandipeputsa Ine, nudzitengera mkazi wa Uriya Mhiti akhale mkazi wako.

11. Atero Yehova, Taona ndidzakuutsira zoipa, zobadwa m'nyumba yako ya iwe wekha; ndipo ndidzacotsa akazi ako pamaso pako ndi kuwapatsa mnansi wako, amene adzagona ndi akazi ako dzuwa liri denene.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 12