Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 11:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. nauza mthengawo kuti, Utatsiriza kuuza mfumu zonse za nkhondozo;

20. kudzali kuti ukapsa mtima wa mfumu nikati kwa iwe, Cifukwa ninji munayandikira pafupi potere pamudzi kukamenyana nao? Simunadziwa kodi kuti apalingawo adzaponya?

21. Ndani anakantha Abimeleki mwana wa Jerubeseti? Sadamponyera kodi mphero mkazi wa palinga nafa iye ku Tebezi? Munasendera bwanji pafupi potere pa lingalo? Tsono udzanena, Mnyamata wanu Uriya Mhiti, iyenso adafa,

22. Comweco mthengawo unamuka, nufika, nudziwitsa Davide zonse Yoabu anamtumiza.

23. Ndipo mthengawo unati kwa Davide, Anthuwo anatilaka naturukira kwa ife kumundako, koma tinawa gwera kufikira polowera kucipata,

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 11