Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 11:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndi m'kalatamo analemba kuti, Mumuike Uriya pa msongwe wa nkhondo yolimba, ndipo mumlekerere kuti akanthidwe nafe.

16. Ndipo Yoabu atayang'anira mudziwo, anaika Uriye pomwe anadziwa kuti pali ngwazi.

17. Ndipo akumudziwo anaturuka, namenyana ndi Yoabu; ndipo adagwapo anthu ena, ndiwo a anyamata a Davide; ndi Uriya Mhiti anafanso.

18. Pamenepo Yoabu anatumiza munthu nauza Davide zonse za nkhondoyi;

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 11