Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 10:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo Hadarezeri anatumiza mthenga nakatenga Aaramu a ku tsidya la cimtsinje; iwo nafika ku Helamu, ndi Sobaki kazembe wa khamu la nkhondo la Hadarezeri anawatsogolera.

17. Ndipo wina anauza Davide; iye nasonkhanitsa Aisrayeli onse, naoloka Yordano nafika ku Helemu, Ndipo Aaramu anandandalitsa nkhondo yao pa Davide namenyana naye.

18. Ndipo Aaramu anathawa pamaso pa Israyeli; Davide naphapo Aaramu apamagareta mazana asanu ndi awiri, ndi apakavalo zikwi makumi anai, nakantha Sobaki kazembe wa khamu lao, nafa iye pomwepo.

19. Ndipo pamene mafumu onse, otumikira Hadarezeri, anaona kuti Aisrayeli anawapambana, iwo anapangana mtendere ndi Aisrayeli, nawatumikira, Comweco Aaramu anaopa kuwathandizanso ana a Amoni.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 10