Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 1:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Usacinene ku Gati,Usacibukitse m'makwalala a Asikeloni,Kuti ana akazi a Afilisti angasekere,Kuti ana akazi a osadulidwawo angapfuule mokondwera.

21. Mapiri inu a Giliboa,Pa inu pasakhale mame kapena mvula, kapena minda yakutengako zopereka.Pakuti kumeneko zikopa za amphamvu zinatayika koipa,Cikopa ca Sauli, monga ca wosadzozedwa ndi mafuta.

22. Uta wa Jonatani sunabwerera,Ndipo lupanga la Sauli silinabwecera cabe,Pa mwazi wa ophedwa, pa mafuta a amphamvuwo.

23. Sauli ndi Jonatani anali okoma ndi okondweretsa m'miyoyo yao,Ndipo m'imfa yao sanasiyana; Anali nalo liwiro loposa ciombankanga,Anali amphamvu koposa mikango.

24. Ana akazi inu a Israyeli, mulirire Sauli,Amene anakubvekani ndi zofira zokometsetsa,Amene anaika zokometsetsa zagolidi pa zobvala zanu.

25. Ha! amphamvuwo anagwa pakati pa nkhondo!Jonatani anaphedwa pamisanje pako.

26. Ndipsinjika mtima cifukwa ca iwe, mbale wanga Jonatani;Wandikomera kwambiri;Cikondi cako, ndinadabwa naco,Cinaposa cikondi ca anthu akazi.

27. Ha! amphamvuwo anagwa,Ndi zida za nkhondo zinaonengeka,

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 1