Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 9:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo zikho zomwera zonse za Solomo zinali zagolidi, ndi zipangizo zonse za nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano zinali za golidi woona; siliva sanayesedwa kanthu m'masiku a Solomo.

21. Pakuti zombo za mfumu zinayenda ku Tarisi ndi anyamata a Huramu; zombo za ku Tarisi zinadza kamodzi zitapita zaka zitatu, ndi kubwera nazo golidi, ndi siliva, minyanga, ndi apusi, ndi mbalame za zitsukwa zazitali za mawanga mawanga.

22. Mamwemo mfumu Solomo inaposa mafumu onse a pa dziko lapansi, kunena za cuma ndi nzeru.

23. Ndipo mafumu onse a pa dziko lapansi anafuna nkhope ya Solomo, kudzamva nzeru zace Mulungu adazilonga m'mtima mwace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 9