Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 6:39-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. pamenepo mumvere Inu m'Mwamba mokhala Inumo pemphero lao ndi pembedzero lao, ndi kulimbitsa mlandu wao; nimukhululukire anthu anu amene anakucimwirani.

40. Tsopano Mulungu wanga, maso anu akhale cipenyere, ndi makutu anu cimvere, pemphero locitika pamalo pano.

41. Ndipo tsopano nyamukani, Yehova Mulungu, kudza kopumulira kwanu, Inu ndi likasa la mphamvu yanu; ansembe anu, Yehova Mulungu, abvale cipulumutso; ndi okondedwa anu akondwere nazo zabwino.

42. Yehova Mulungu, musabweza nkhope ya wodzozedwa wanu, mukumbukile zacifundo za Davide mtumiki wanu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 6