Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 6:35-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. pamenepo mumvere m'Mwamba pemphero lao ndi pembedzero lao, ndi kulimbitsa mlandu wao.

36. Akacimwira Inu (pakuti palibe munthu wosacimwa), nimukakwiya nao, ndi kuwapereka kwa adani, kuti awatenge andende kumka nao ku dziko lakutali, kapena lapafupi;

37. koma akalingirira m'mtima mwao kudziko kumene anawatengera andende, nakatembenuka, nakapembedzera Inu m'dziko la undende wao, ndi kuti, Tacimwa, tacita mphulupulu, tacita coipa;

38. akabwerera kwa Inu ndi mtima wao wonse, ndi moyo wao wonse, m'dziko la undende wao, kumene adawatengera andende; nakapemphera kuloza ku dziko lao limene munapatsa makolo ao, ndi mudzi mudausankha, ndi kunyumba ndamangira dzina lanuyi;

39. pamenepo mumvere Inu m'Mwamba mokhala Inumo pemphero lao ndi pembedzero lao, ndi kulimbitsa mlandu wao; nimukhululukire anthu anu amene anakucimwirani.

40. Tsopano Mulungu wanga, maso anu akhale cipenyere, ndi makutu anu cimvere, pemphero locitika pamalo pano.

41. Ndipo tsopano nyamukani, Yehova Mulungu, kudza kopumulira kwanu, Inu ndi likasa la mphamvu yanu; ansembe anu, Yehova Mulungu, abvale cipulumutso; ndi okondedwa anu akondwere nazo zabwino.

42. Yehova Mulungu, musabweza nkhope ya wodzozedwa wanu, mukumbukile zacifundo za Davide mtumiki wanu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 6