Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 4:9-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Anamanganso bwalo la ansembe, ndi bwalo lalikuru, ndi zitseko za kubwalo, nakuta zitseko zace ndi mkuwa.

10. Ndipo anaika thawalelo ku dzanja lamanja la nyumba kum'mawa cakumwela.

11. Ndipo Huramu anapanga miphika, ndi zoolera zace, ndi mbale zowazira zace. Natsiriza Huramu nchito adaicitira mfumu Solomo m'nyumba ya Mulungu:

12. nsanamira ziwiri, ndi zikhozo, ndi mitu iwiri inali pamwamba pa nsanamirazo, ndi maukonde awiri akukuta zikho ziwiri za mitu iri pamwamba pa nsanamirazo,

13. ndi makangaza mazana anai a maukonde awiri wa; mizere iwiri ya makangaza ya ukonde uli wonse, akukuta zikho ziwiri za mitu, inali pa nsanamirazo.

14. Anapanganso maphaka, napanga mbiya zamphwamphwa khumi pamwamba pa maphaka;

15. thawale limodzi ndi ng'ombe khumi ndi ziwiri pansi pace.

16. Miphika yomwe, ndi zoolera, ndi mitungo, ndi zipangizo zace zonse, Huramu Abi anazipangira mfumu Solomo, kuzipangira nyumba ya Yehova, za mkuwa wonyezimira.

17. Mfumuyi inaziyenga pa cidikha ca ku Yordano, m'dothi ladongo, pakati pa Sukoti ndi Zereda.

18. Ndipo Solomo anazipanga zipangizo izi zonse zocurukadi, pakuti kulemera kwace kwa mkuwa sikunayeseka.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 4