Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 34:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo pakuturutsa ndarama zimene adalowa nazo ku nyumba ya Yehova, Hilikiya wansembe anapeza buku la cilamulo la Yehova mwa dzanja la Mose.

15. Ndipo Hilikiya anayankha nati kwa Safani mlembi, Ndapeza buku la cilamulo m'nyumba ya Yehova. Hilikiya napereka buku kwa Safani.

16. Ndi Safani anamuka nalo buku kwa mfumu, nabwezeranso mau kwa mfumu, ndi kuti, Zonse mudazipereka kwa anyamata anu alikuzicita.

17. Nakhuthula ndarama zinapezeka m'nyumba ya Yehova, nazipereka m'manja a akapitao ndi m'manja a anchito.

18. Ndipo Safani mlembi anauza mfumu, ndi kuti, Hilikiya wansembe anandipatsa buku. Nawerengamo Safani pamaso pa mfumu.

19. Ndipo kunali, atamva mfumu mau a cilamulo, anang'amba zobvala zace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 34