Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 33:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Pemphero lace lomwe, ndi m'mene Mulungu anapembedzeka naye, ndi chimo lace lonse, ndi kulakwa kwace, ndi apo anamanga misanje, naimika zifanizo ndi mafano osema asanadzicepetse, taonani, zalembedwa m'buku la mau a Hozai.

20. Momwemo Manase anagona ndi makolo ace, namuika m'nyumba mwace mwace; ndi Amoni mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

21. Amoni ndiye wa zaka makumi awiri mphambu ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka ziwiri.

22. Ndipo anacita coipa pamaso pa Yehova, monga umo anacitira Manase atate wace; pakuti Amoni anaphera nsembe mafano osema onse amene adawapanga Manase atate wace, nawatumikira.

23. Koma sanadzicepetsa pamaso pa Yehova, monga umo anadzicepetsera Manase atate wace; koma Amoni amene anacurukitsa kuparamula kwace.

24. Ndipo anyamata ace anampangira ciwembu, namupha m'nyumba yace yace.

25. Koma anthu a m'dziko anapha onse adampangira ciwembu mfumu Amoni; ndi anthu a m'dziko analonga Yosiya mwana wace akhale mfumu m'malo mwace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 33