Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 33:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi asanu mphambu zisanu.

2. Nacita coipa pamaso pa Yehova, monga mwa zonyansa za amitundu, amene Yehova anawacotsa m'dziko mwao pamaso pa ana a Israyeli.

3. Pakuti anamanganso misanje adaipasula Hezekiya atate wace, nautsira Abaala maguwa a nsembe, napanga zifanizo, nalambira khamu lonse la kuthambo, nalitumikira.

4. Namanga maguwa a nsembe m'nyumba ya Yehova, imene Yehova adati, M'Yerusalemu mudzakhala dzina langa ku nthawi zonse.

5. Namangiranso khamu lonse la kuthambo maguwa a nsembe m'mabwalo awiri a nyumba ya Yehoya.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 33