Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 32:32-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Macitidwe ena tsono a Hezekiya, ndi nchito zace zokoma, taonani, zilembedwa m'masomphenya a Yesaya mneneri mwana wa Amozi, ndi m'buku la mafumu a Yuda ndi Israyeli.

33. Ndipo Hezekiya anagona ndi makolo ace, namuika polowerera ku manda a ana a Davide; ndi Ayuda onse ndi okhala m'Yerusalemu anamcitira ulemu pa imfa yace. Ndipo Manase mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 32