Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 3:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndi likole linali kukhomo kwa nyumba, m'litali mwace monga mwa kupingasa kwa nyumba munali mikono makumi awiri, ndi msinkhu wace zana limodzi mphambu makumr awiri; ndipo analikuta m'katimo ndi golidi woona.

5. M'nyumba yaikuru tsono anacinga ndi mitengo yamlombwa, imene anaikuta ndi golidi wabwino, nalembapo ngati migwalangwa ndi maunyolo.

6. Ndipo anakuta nyumba ndi miyala ya mtengo wace; ndi golidi wace ndiye golidi wa Parivaimu.

7. Anamamatizanso kacisi, mitanda, ziundo, ndi makoma ace, ndi zitseko zace, ndi golidi; nalemba akerubi pamakoma.

8. Ndipo anamanga malo opatulikitsa, m'litali mwace monga mwa kupingasa kwa nyumba mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwace mikono makumi awiri; naikuta ndi golidi wabwino wakufikira matalente mazana asanu ndi limodzi.

9. Ndi kulemera kwace kwa misomali ndiko masekeli makumi asanu a golidi. Ndipo anazikuta ndi golidi zipinda zosanjikizana.

10. Ndipo m'malo opatulikitsa anapanga akerubi awiri, anacita osema, nawakuta ndi golidi.

11. Ndi mapiko a akerubi m'litali mwace ndimo mikono makumi awiri; phiko la kerubi mmodzi mikono isanu, lojima khoma la nyumba; ndi phiko linzace mikono isanu, lokhudzana nalo phiko la kerubi wina.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 3