Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 3:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Solomo anayamba kumanga nyumba ya Yehova ku Yerusalemu, m'phiri la Moriya, kumene Mulungu anaonekera kwa Davide atate wace, pamalo pamene Davide anakonzeratu pa dwale la Orinani Myebusi.

2. Nayamba kumanga tsiku laciwiri la mwezi waciwiri, caka cacinai ca ufumu wace.

3. Ndipo maziko adawaika Solomo akumangapo nyumba ya Mulungu ndi awa: utali wace, kuyesa mikono monga mwa muyeso wakale, ndiwo mikono makumi asanu ndi limodzi, ndi kupingasa kwace mikono makumi awiri.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 3