Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 26:11-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Uziya anali nalonso khamu la anthu a nkhondo, oturuka kunkhondo magulu; nawawerenga monga mwa mawerengedwe ao ndi dzanja la mlembi Yeyeli, ndi kapitao Maseya, monga anawauza Hananiya kazembe wina wa mfumu.

12. Ciwerengo conse ca akuru a nyumba za makolo, ndiwo ngwazi zamphamvu, ndico zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi limodzi.

13. Ndipo m'dzanja mwao munali khamu la nkhondo zikwi mazana atatu mphambu zikwi zisanu ndi ziwiri kudza mazana asanu ocita nkhondo ndi mphamvu yaikuru, kuthandiza mfumu alimbane ndi adani.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 26