Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 25:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Amaziya anali wa zaka makumi awiri mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi awiri mphambu zisanu ndi zinai; ndi dzina la mace ndiye Yehoadana wa ku Yerusalemu.

2. Ndipo anacita zoongoka pamaso pa Yehova, koma wosacita ndi mtima wangwiro.

3. Kunacitika tsono, utamkhazikikira ufumu, anapha anyamata ace amene adapha mfumu atate wace.

4. Koma sanapha ana ao, koma anacita monga umo mulembedwa m'cilamulo, m'buku la Mose, monga Yehova analamulira, ndi kuti, Atate asafere ana, ndi ana asafere atate; koma yense afere chimo lace lace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 25