Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 20:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. nakhala m'mwemo iwowa, nakumangirani m'mwemo malo opatulika a dzina lanu, ndi kuti,

9. Cikatigwera coipa, lupanga, ciweruzo, kapena mliri, kapena njala, tidzakhala ciriri pakhomo pa nyumba iyi, ndi pamaso panu, (pakuti m'nyumba muno muli dzina lanu), ndi kupfuulira kwa Inu m'kusauka kwathu; ndipo mudzamvera ndi kulanditsa.

10. Ndipo tsopano, taonani ana a Amoni, ndi Moabu, ndi a ku phiri la Seiri, amene simunalola Israyeli awalowere, pakuturuka iwo m'dziko la Aigupto, koma anawapambukira osawaononga;

11. tapenyani, m'mene atibwezera; kudzatiinga m'colowa canu, cimene munatipatsa cikhale colowa cathu.

12. Mulungu wathu, simudzawaweruza? pakuti mwa ife mulibe mphamvu yakulimbana nao aunyinji ambiri awa akutidzera; ndipo sitidziwa ngati tidzatani, koma maso athu ali kwa Inu.

13. Ndipo Ayuda onse anakhala ciriri pamaso pa Yehova, pamodzi ndi makanda ao, akazi ao, ndi ana ao.

14. Pamenepo mzimu wa Yehova unagwera Yahazieli mwana wa Zekriya, mwana wa Benaya, mwana wa Yetieli, mwana wa Mataniya, Mlevi, wa ana a Asafu, pakati pa msonkhano;

15. nati iye, Tamverani Ayuda inu nonse, ndi inu okhala m'Yerusalemu, ndi inu mfumu Yehosafati, atero nanu Yehova, Musaope musatenge nkhawa cifukwa ca aunyinji ambiri awa; pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 20