Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 16:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi cimodzi ca Asa, Basa mfumu ya Israyeli anakwera kulimbana ndi Yuda, namangitsa Rama, kuwaletsa anthu asaturuke kapena kulowa kwa Asa mfumu ya Yuda.

2. Pamenepo Asa anaturutsa siliva ndi golidi ku cuma ca nyumba ya Yehova, ndi ca nyumba ya mfumu; nazitumiza kwa Benihadadi mfumu ya Aramu, yokhala ku Damasiko, ndi kuti,

3. Pakhale pangano pakati pa ine ndi inu, monga pakati pa atate wange ndi atate wanu; taonani, ndakutumizirani siliva ndi golidi; mukani, pasulani pangano lanu ndi Basa mfumu ya Israyeli, kuti andicokere.

4. Ndipo Benihadadi anamvera mfumu Asa natumiza akazembe a magulu ace a nkhondo ayambane ndi midzi ya Israyeli, nakantha Iyoni, ndi Dani, ndi Abelimaimu, ndi midzi yonse ya cuma ya Nafitali,

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 16