Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 14:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Momwemo Abiya anagona ndi makolo ace, ndipo anamuika m'mudzi wa Davide; ndi Asa mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace, m'masiku ace dziko linaona bata zaka khumi.

2. Ndipo Asa anacita cokoma ndi coyenera m'maso mwa Yehova Mulungu wace,

3. nacotsa maguwa a nsembe acilendo, ndi misanje; naphwanya zoimiritsa zao, nalikha zifanizo zao,

4. nauza Yuda afune Yehova Mulungu wa makolo ao, ndi kucita cilamulo ndi cowauza, Iye.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 14