Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 13:16-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo ana a Israyeli anathawa pamaso pa Yuda, nawapereka Mulungu m'dzanja lao.

17. Ndipo Abiya ndi anthu ace anawakantha makanthidwe akuru; nagwa, nafa amuna osankhika zikwi mazanaasanu a Israyeli.

18. Momwemo anacepetsedwa ana a Israyeli nthawi ija, nalakika ana a Yuda; popeza anatama Yehova Mulungu wa makolo ao.

19. Ndipo Abiya analondola Yerobiamu, namlanda midzi yace, Beteli ndi miraga yace, ndi Yesana ndi miraga yace, ndi Efroni ndi miraga yace.

20. Ndi Yerobiamu sanaonanso mphamvu m'masiku a Abiya, namkantha Yehova, wa iye.

21. Koma Abiya anakula mphamvu, nadzitengera akazi khumi ndi anai, nabala ana amuna makumi awiri mphambu awiri, ndi ana akazi khumi mphambu asanu ndi mmodzi.

22. Macitidwe ena tsono a Abiya, ndi mayendedwe ace, ndi mau ace, alembedwa m'buku lomasulira la mneneri Ido.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 13