Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 11:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. ndi Gati, ndi Maresa, ndi Zifi,

9. ndi Adoraimu, ndi Lakisi, ndi Azeka,

10. ndi Zora, ndi Ayaloni, ndi Hebroni; ndiyo midzi yamalinga ya m'Yuda ndi Benjamini.

11. Ndipo analimbitsa malingawo, naikamo atsogoleri, ndi cakudya cosungikiratu, ndi mafuta, ndi lvinyo.

12. Ndi m'midzi iri yonse anaikamo zikopa ndi mikondo, nailimbitsa cilimbitsire. Ndipo Yuda ndi Benjamini anakhala ace.

13. Ndipo ansembe ndi Alevi okhala m'Israyeli lonse anadziphatikiza kwa iye, ocokera m'malire ao Onse.

14. Pakuti Alevi anasiya podyetsa pao, ndi maiko ao ao, nadza ku Yuda ndi ku Yerusalemu; popeza Yerobiamu ndi ana ace anawataya, kuti asacitire Yehova nchito ya nsembe;

15. nadziikira ansembe a misanje, ndi a ziwanda, ndi a ana a ng'ombe adawapanga.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 11