Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 9:31-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Ndipo polowa Yehu pacipata, mkaziyo anati, Mtendere kodi Zimri, iwe wakupha mbuyako?

32. Koma anakweza maso ace kuzenera, nati, Ali ndi ine ndani? Ndani? Nampenyererako adindo awiri kapena atatu.

33. Nati iye, Mgwetsereni pansi. Namgwetsera pansi, nuwazikako mwazi wace pakhoma ndi pa akavalo, nampondereza iye pansi.

34. Ndipo atalowa, anadya namwa, nati, Kampenyeni tsono mkazi wotembereredwa uyu, nimumuike; popeza ndiye mwana wa mfumu.

35. Namuka iwo kuti amuike; koma sanapezako kanthu kena koma bade, ndi mapazi, ndi zikhato za manja.

36. Nabwerera iwo, namfotokozera. Nati iye, Ndiwo mau a Yehova ananena wo mwa mtumiki wace Eliya wa ku Tisibe, ndi koti, Pa munda wa Yezreeli agaru adzadya mnofu wa Yezebeli;

37. ndi thupi la Yezebeli lidzakhala ngati ndowe pamunda m'dera la Yezreeli, kuti sadzati, Ndi Yezebeli uyu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 9