Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 9:25-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Nati Yehu kwa Bidikara kazembe wace, Mnyamule, numponye m'munda wa Naboti wa ku Yezreeli; pakuti kumbukila m'mene ine ndi iwe tinali pa akavalo athu pamodzi kutsata Ahabu atate wace, Yehova anamsenzetsa katundu uyu.

26. Ndapenyadi dzulo mwazi wa Naboti ndi mwazi wa ana ace, ati Yehova; ndipo ndikubwezera pamunda pano, ati Yehova, Mtengeni tsono, mumponye pamundapo, monga mwa mau a Yehova.

27. Koma pociona ici Ahaziya mfumu ya Yuda anathawa njira ya ku khumbi la m'munda. Namtsata Yehu, nati, Mumkanthe uyonso pagareta; namkantha pa cikweza ca Guru ciri pafupi pa Yibleamu. Nathawira iye ku Megido, namwalira komweko.

28. Ndipo anyamata ace anamnyamulira pagareta kumka naye ku Yerusalemu, namuika ku manda ace pamodzi ndi makolo ace m'mudzi wa Davide.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 9