Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 8:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Masiku ace Aedomu anapanduka ku ulamuliro wa Yuda, nadziikira mfumu okha.

21. Pamenepo Yoramu anaoloka kumka ku Zairi, ndi magareta ace onse pamodzi naye; nauka iye usiku, nakantha Aedomu akumzinga ndi nduna za magareta, nathawira anthu ku mahema ao.

22. Motero Aedomu anapanduka ku ulamuliro wa Yuda mpaka lero lino. Ndipo Alibina anapanduka nthawi yomweyi.

23. Ndi macitidwe ena a Yoramu, ndi zonse anazicita, sizinalembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda.

24. Nagona Yoramu ndi makolo ace, naikidwa pamodzi ndi makolo ace m'mudzi wa Davide; ndipo Ahaziya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

25. Caka cakhumi ndi ziwiri ca Yoramu mwana wa Ahabu mfumu Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda analowa ufumu wace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 8