Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 8:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo anacoka kwa Elisa, nadza kwa mbuye wace; ameneyo ananena naye, Anakuuza ciani Elisa? Nati iye, Anandiuza kuti mudzacira ndithu.

15. Ndipo kunali m'mawa mwace, anatenga cimbwi, nacibviika m'madzi, naciphimba pankhope pa mfumu, nifa; ndipo Hazaeli analowa ufumu m'malo mwace.

16. Ndipo caka cacisanu ca Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israyeli, pokhala Yehosafati mfumu ya Yuda, Yehoramu mwana wa Yehosafati analowa ufumu.

17. Ndiye wa zaka makumi atatu ndi ciwiri polowa ufumu wace, nacita ufumu zaka zisanu ndi zitatu ku Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 8