Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 5:23-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Nati Namani, Viole ulandire matalente awiri. Namkangamiza namanga matalente awiri a siliva m'matumba awiri, ndi zobvala zosintha ziwiri, nasenzetsa anyamata ace awiri; iwo anatsogola atazisenza.

24. Ndipo pamene anafika kumsanje anazilandira m'manjamwao, naziika m'nyumba; nauza anthuwo amuke, iwo nacoka.

25. Pamenepo analowa, na, ima kwa mbuye wace. Ndipo Elisa ananena naye, Ufuma kuti Gehazi? Nati, Ngati mnyamata wanu wayenda konse?

26. Ndipo anati kwa iye, Mtima wanga sunakuperekeza kodi, umo munthuyo anatembenuka pa gareta wace kukomana ndi iwe? Kodi nyengo yino ndiyo yakulandira siliva, ndi kulandira zobvala, ndi minda yaazitona, ndi yampesa, ndi nkhosa, ndi ng'ombe, ndi akapolo; ndi adzakazi?

27. Cifukwa cace khate la Namani lidzakumamatira iwe ndi mbumba yako cikhalire. Ndipo anaturuka pamaso pace wakhate wa mbu ngati cipale cofewa.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 5